Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo 3

Mawu Ofotokoza Chigawo 3

Baibulo limanena kuti Chigumula chitatha, panali anthu ena omwe ankatumikira Yehova. Ena mwa anthuwa anali Abulahamu amene ankadziwika kuti anali mnzake wa Yehova. N’chifukwa chiyani Abulahamu ankatchedwa mnzake wa Yehova? Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kudziwa kuti Yehova amamukonda kwambiri ndipo amafunitsitsa kumuthandiza. Mofanana ndi Abulahamu komanso anthu ena okhulupirika monga Loti ndi Yakobo, tingathe kupempha Yehova kuti atithandize. Komanso tizikhulupirira kuti Yehova adzachita chilichonse chimene wanena.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 7

Nsanja ya ku Babele

Anthu anaganiza zomanga mzinda wokhala ndi nsanja yaitali mpaka kumwamba. N’chifukwa chiyani Mulungu anawapangitsa kuti mwadzidzidzi ayambe kulankhula zinenero zosiyanasiyana?

MUTU 8

Abulahamu ndi Sara Anamvera Mulungu

N’chifukwa chiyani Abulahamu ndi Sara anasiya mzinda wolemera wa Uri n’kumakakhala ngati alendo ku Kanani?

MUTU 9

Anakhala Ndi Mwana Atakalamba

Kodi Mulungu anakwaniritsa bwanji lonjezo lake kwa Abulahamu? Kodi analikwaniritsa kudzera mwa mwana uti, Isaki kapena Isimaeli?

MUTU 10

Kumbukirani Mkazi wa Loti

Mulungu anachititsa kuti moto ndi sulufule zigwere mumzinda wa Sodomu ndi wa Gomora. N’chifukwa chiyani mizindayi inawonongedwa? N’chifukwa chiyani tiyenera kukumbukira mkazi wa Loti?

MUTU 11

Abulahamu Anasonyeza Kuti Anali Wokhulupirika

Mulungu anauza Abulahamu kuti: ‘Chonde, tenga mwana wako mmodzi yekhayo kuti ukamupereke nsembe paphiri la Moriya.’ Kodi pamenepa Abulahamu akanatani?

MUTU 12

Yakobo Analandira Madalitso

Isaki ndi Rebeka anali ndi ana awiri amapasa ndipo mayina awo anali Esau ndi Yakobo. Esau anali wamkulu ndipo ankayenera kulandira madalitso. N’chifukwa chiyani anasinthanitsa madalitsowo ndi mbale ya mphodza?

MUTU 13

Yakobo ndi Esau Anagwirizananso

Kodi Yakobo anatani kuti mngelo amudalitse? Nanga anatani kuti akhululukirane ndi Esau?