Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo 4

Mawu Ofotokoza Chigawo 4

Chigawochi chikufotokoza nkhani ya Yosefe, Yobu, Mose komanso Aisiraeli. Onsewa anapirira mayesero osiyanasiyana ochokera kwa Mdyerekezi. Ena mwa anthuwa anachitiridwa zinthu zopanda chilungamo, kuikidwa m’ndende ngakhalenso kuphedwa kumene. Koma Yehova anawateteza m’njira zosiyanasiyana. Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kumvetsa mmene atumiki a Yehova amenewa anavutikira koma n’kukhalabe okhulupirika.

Yehova anagwiritsa ntchito Miliri 10 pofuna kusonyeza kuti iyeyo ndi wamphamvu kwambiri kuposa milungu ya Aiguputo. Fotokozani mmene Yehova anatetezera anthu ake m’mbuyomu komanso mmene akuwatetezera masiku ano.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 14

Kapolo Amene Ankamvera Mulungu

Yosefe ankachita zabwino koma anavutika kwambiri. N’chifukwa chiyani?

MUTU 15

Yehova Sanamuiwale Yosefe

Ngakhale kuti Yosefe anali kutali ndi achibale ake, Yehova anali naye.

MUTU 16

Kodi Yobu Anali Ndani?

Yobu ankamvera Yehova ngakhale zinthu zitavuta.

MUTU 17

Mose Anasankha Kuti Azilambira Yehova

Mose ali mwana anapulumuka chifukwa cha nzeru za mayi ake.

MUTU 18

Anaona Chitsamba Chikuyaka

N’chifukwa chiyani chitsamba chinkayaka koma osapsa?

MUTU 19

Miliri Itatu Yoyambirira

Farao anabweretsera anthu ake mavuto chifukwa anali wonyada ndipo anakana kuti anthu a Mulungu apite.

MUTU 20

Miliri Inanso 6

Kodi miliri imeneyi inasiyana bwanji ndi itatu yoyamba ija?

MUTU 21

Mliri wa 10

Mliri umenewu unali wopweteka kwambiri moti Farao analola kuti Aisiraeli apite.

MUTU 22

Pa Nyanja Yofiira Panachitika Zodabwitsa Kwambiri

Farao sanafe ndi miliri 10. Koma kodi anapulumukanso pa chozizwitsa cha pa Nyanja Yofiirachi?