Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mawu Oyamba a Cigawo 4

Mawu Oyamba a Cigawo 4

Cigawo cino cifotokoza za Yosefe, Yobu, Mose, komanso Aisiraeli. Onsewa anavutika kwambili cifukwa ca Mdyelekezi. Ena anacitilidwa zopanda cilungamo, kuponyewa m’ndende, kuikidwa ukapolo, ngakhale kufedwa okondedwa awo mwadzidzidzi. Ngakhale n’telo, Yehova anawateteza m’njila zolekana-lekana. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kumvetsa mmene atumiki a Yehova anavutikila, koma osataya cikhulupililo cawo.

Yehova anaseŵenzetsa Milili 10 kuonetsa kuti iye ni wamphamvu ngako kupambana milungu yonse ya Aiguputo. Fotokozani mmene Yehova anatetezela anthu ake kumbuyoko, na mmene amawatetezela masiku ano.

M'CIGAWO CINO

PHUNZILO 14

Kapolo Amene Anamvela Mulungu

Yosefe anali kucita zabwino, koma anakumanabe na mavuto aakulu. Cifukwa ciani?

PHUNZILO 15

Yehova Sanamuiŵalepo Yosefe

Ngakhale kuti Yosefe anali kutali na banja lake, Mulungu anaonetsa kuti anali naye.

PHUNZILO 16

Kodi Yobu Anali Ndani?

Anamvela Yehova ngakhale kuti zinali zovuta.

PHUNZILO 17

Mose Anasankha Kulambila Yehova

Ali mwana, Mose anapulumuka cifukwa amayi ake anacita zinthu mwanzelu.

PHUNZILO 18

Citsamba Coyaka Moto

N’cifukwa ciani citsamba sicinali kupsa na moto?

PHUNZILO 19

Milili Itatu Yoyambilila

Farao anabweletsa mavuto pa anthu ake. Cifukwa conyada, anakana kucita cinthu cosavuta.

PHUNZILO 20

Milili 6 Yokonkhapo

Kodi milili imeneyi inasiyana bwanji na itatu yoyambilila?

PHUNZILO 21

Mlili wa Namba 10

Mlili umenewu unali woopsa kwambili cakuti Farao wonyadayo anagonja.

PHUNZILO 22

Cozizwitsa pa Nyanja Yofiila

Farao anapulumuka milili 10. Koma kodi anapulumuka cozizwitsa ici ca Mulungu?