Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mawu Oyamba a Cigawo 5

Mawu Oyamba a Cigawo 5

Patapita miyezi iŵili, Aisiraeli atawoloka Nyanja Yofiila, anafika pa Phili la Sinai. Pamalo amenewo, Yehova anacita pangano na mtundu wa Isiraeli kuti adzakhala mtundu wake wapadela. Iye anawateteza na kuwapatsa zonse zofunikila monga cakudya ca mana, zovala zimene sizinali kutha, komanso malo okhala otetezeka. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kumvetsa cifukwa cake Yehova anapatsa Aisiraeli Cilamulo, cihema colambililako, komanso ansembe. Gogomezani kufunika kocita zimene talonjeza, kukhala odzicepetsa, na kukhala okhulupilika kwa Yehova nthawi zonse.

M'CIGAWO CINO

PHUNZILO 23

Lonjezo kwa Yehova

Aisiraeli anacita pangano lapadela kwa Mulungu atamanga misasa pafupi na Phili la Sinai.

PHUNZILO 24

Anaphwanya Lonjezo Lawo

Pamene Mose anali kulandila Mamulo 10, Aisiraeli anacita chimo lalikulu.

PHUNZILO 25

Cihema Colambililako

M’cihema capadela cimeneci munali likasa la cipangano.

PHUNZILO 26

Azondi 12

Yoswa na Kalebe anali osiyana ndi amuna ena 10 amene anazonda dziko la Kanani.

PHUNZILO 27

Anapandukila Yehova

Kora, Datani, Abiramu, na anthu ena 250 analephela kuzindikila mfundo yofunika yokhudza Yehova.

PHUNZILO 28

Bulu wa Balamu Akamba

Bulu anaona wina wake amene Balamu sanamuone.