Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo 7

Mawu Ofotokoza Chigawo 7

Chigawochi chikufotokoza mbiri ya moyo wa Mfumu Sauli komanso Mfumu Davide. Mbiriyi inachitika pafupifupi kwa zaka 80. Poyamba Sauli anali wodzichepetsa komanso ankamvera Mulungu. Koma kenako anasintha n’kusiya kutsatira malangizo a Yehova. Zitatero Yehova anamukana ndipo patapita nthawi anauza Samueli kuti adzoze Davide kuti akhale mfumu. Sauli ankachitira nsanje Davide ndipo mobwerezabwereza anayesa kuti amuphe koma Davideyo sanabwezere. Mwana wa Sauli dzina lake Yonatani, ankadziwa kuti Davide wasankhidwa ndi Yehova choncho anakhala wokhulupirika kwa Davideyo. Davide anachita machimo ena akuluakulu koma nthawi zonse ankamvera Yehova akamudzudzula. Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanu kuti aziona kufunika kotsatira malangizo a Mulungu nthawi zonse.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 39

Mfumu Yoyamba ya Aisiraeli

Mulungu anapatsa Aisiraeli oweruza oti aziwatsogolera koma iwo anapempha kuti akhale ndi mfumu. Samueli anadzoza Sauli kuti akhale mfumu yoyamba koma kenako Yehova anakana Sauliyo. Kodi mukudziwa chifukwa chake?

MUTU 40

Davide Anapha Goliyati

Yehova anasankha Davide kuti adzakhale mfumu yotsatira ya Aisiraeli, ndipo zimene Davide anachita zinasonyeza kuti Yehova anasankha bwino.

MUTU 41

Davide ndi Sauli

N’chifukwa chiyani Sauli ankadana ndi Davide, nanga Davideyo anatani?

MUTU 42

Yonatani Anali Wolimba Mtima Komanso Wokhulupirika

Mwana wa mfumu anakhala mnzake wapamtima wa Davide.

MUTU 43

Tchimo la Mfumu Davide

Zimene Davide anachita zinabweretsa mavuto aakulu.