Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Mawu Oyamba a Cigawo 9

Mawu Oyamba a Cigawo 9

M’cigawo cino tidzaphunzila za acicepele, aneneli, komanso mafumu amene anaonetsa cikhulupililo camphamvu mwa Yehova. Ku Siriya, kunali kamtsikana kena kaciisiraeli komwe kanali kukhulupilila kuti mneneli wa Yehova angacilitse Namani. Mneneli Elisa anali na cidalilo conse mwa Yehova kuti adzam’teteza ku gulu la adani ake. Mkulu wa Ansembe Yehoyada anaika moyo wake paciswe, kuti ateteze wacicepele Yehoasi kwa ambuye ake aakazi oipa kwambili, Ataliya. Mfumu Hezekiya inali na cidalilo cakuti Yehova adzapulumutsa Yerusalemu, ndipo iye sanagonje kwa Asuri pomuwopseza. Mfumu Yosiya inafafaniza kulambila mafano m’dziko lawo, inamanganso kacisi, na kuthandiza anthu kuyambanso kulambila koona.

M'CIGAWO CINO

PHUNZILO 51

Kamtsikana Kathandiza Mkulu wa Asilikali

Kamtsikana kaciisiraeli kauza adona ake za mphamvu zazikulu za Yehova za kucilitsa mozizwitsa.

PHUNZILO 52

Asilikali a Yehova Amoto

Mmene mtumiki wa Elisa anaonela kuti ‘tili na ambili kumbali yathu kuposa amene ali kumbali yawo.’

PHUNZILO 53

Yehoyada Anali Wolimba Mtima

Mosasamala kanthu za mfumukazi yoipa, wansembe wokhulupilika aonetsa kulimba mtima.

PHUNZILO 54

Yehova Anamulezela Mtima Yona

Kodi cinacitika n’ciani kuti mmodzi wa aneneli a Mulungu amezedwe na cinsomba cacikulu? Nanga anacokamo bwanji? Kodi Yehova anam’phunzitsa ciani?

PHUNZILO 55

Mngelo wa Yehova Ateteza Hezekiya

Adani a Ayuda akuti Yehova sadzateteza anthu ake, koma zimenezi si zoona!

PHUNZILO 56

Yosiya Anali Kukonda Cilamulo ca Mulungu

Yosiya akhala mfumu ali na zaka 8 cabe, ndipo athandiza anthu kuyamba kulambila Yehova.