Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 10

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 10

Yehova ndi Mfumu ya chilengedwe chonse. Iye wakhala akulamulira kuyambira kalekale ndipo sadzasiya. Iye anapulumutsa Yeremiya m’chitsime. Anapulumutsanso Sadirake, Mesake ndi Abedinego m’ng’anjo ya moto ndiponso anapulumutsa Danieli m’dzenje la mikango. Iye anatetezanso Esitere n’cholinga choti apulumutse anthu a mtundu wake. Yehova sadzalola kuti zoipa zizingopitirizabe. Ulosi wonena za chifaniziro chachikulu komanso mtengo waukulu umasonyeza kuti Ufumu wa Yehova udzathetsa mavuto onse ndipo udzalamulira dziko lonse.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 57

Yehova Anauza Yeremiya Kuti Azilalikira

Zimene mneneri wachinyamatayu anafotokoza zinakwiyitsa kwambiri akuluakulu a Ayuda.

MUTU 58

Mzinda wa Yerusalemu Unawonongedwa

Ayuda anapitiriza kulambira milungu yonyenga choncho Yehova anawasiya.

MUTU 59

Anyamata 4 Anamvera Yehova

Anyamata achiyuda anakhalabe okhulupirika kwa Yehova ngakhale pamene anali kunyumba yachifumu ku Babulo.

MUTU 60

Ufumu Umene Udzalamulire Mpaka Kalekale

Danieli anafotokoza tanthauzo la maloto odabwitsa a Nebukadinezara.

MUTU 61

Anakana Kulambira Fano

Sadirake, Mesake ndi Abedinego anakana kulambira fano la golide la mfumu ya ku Babulo.

MUTU 62

Ufumu Wofanana ndi Mtengo Waukulu

Maloto a Nebukadinezara anali okhudza tsogolo lake.

MUTU 63

Dzanja Linalemba Pakhoma

Kodi dzanjali linalemba pakhoma pa nthawi iti ndipo zinkatanthauza chiyani?

MUTU 64

Danieli Anaponyedwa M’dzenje la Mikango

Tizipemphera kwa Yehova tsiku lililonse ngati Danieli.

MUTU 65

Esitere Anapulumutsa Anthu a Mtundu Wake

Ngakhale kuti iye anali mlendo m’dzikoli komanso wamasiye anakhala mfumukazi.

MUTU 66

Ezara Ankaphunzitsa Chilamulo cha Mulungu

Aisiraeli atamvetsera zimene Ezara anawawerengera, anapanga lonjezo lapadera kwa Mulungu.

MUTU 67

Mpanda wa Yerusalemu Unamangidwanso

Nehemiya anamva zoti adani akufuna kuwaukira. N’chifukwa chiyani iye sanaope?