Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 12

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 12

Yesu anaphunzitsa anthu zokhudza Ufumu wakumwamba. Iye anawaphunzitsanso kuti azipemphera kuti dzina la Mulungu liyeretsedwe, Ufumu wake ubwere komanso chifuniro chake chichitike padzikoli. Ngati ndinu kholo, fotokozerani mwana wanuyo chifukwa chake pempheroli ndi lofunika kwa ife. Yesu sanalole kuti Satana amulepheretse kukhala wokhulupirika kwa Mulungu. Iye anasankha atumwi ake ndipo iwo ndi amene anali oyamba kusankhidwa kuti adzalamulire nawo mu Ufumu. Ngati ndinu kholo, thandizani mwana wanuyo kuti aone zoti Yesu anali wodzipereka kwambiri pa kulambira koona. Popeza Yesu ankafuna kuthandiza anthu anachiritsa odwala, anadyetsa anjala komanso anaukitsa akufa. Zinthu zodabwitsa zimene anachitazi zinasonyeza zimene Ufumu wa Mulungu udzachitire anthu.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 74

Yesu Anakhala Mesiya

Kodi Yohane ankatanthauza chiyani pamene ananena kuti Yesu ndi Mwanawankhosa wa Mulungu?

MUTU 75

Mdyerekezi Anayesa Yesu

Mdyerekezi anayesa Yesu katatu. Kodi mayesero ake anali otani? Kodi Yesu anatani?

MUTU 76

Yesu Anayeretsa Kachisi

N’chifukwa chiyani Yesu anatulutsa nyama m’kachisi ndiponso anagubuduza matebulo a osintha ndalama?

MUTU 77

Yesu Anakumana ndi Mayi Pachitsime

N’chifukwa chiyani mayi wachisamariya anadabwa kuona kuti Yesu akumulankhula? Kodi Yesu anamuuza mfundo iti yomwe anali asanauze aliyense?

MUTU 78

Yesu Ankalalikira Uthenga wa Ufumu

Yesu anauza ophunzira ake kuti akhala “asodzi a anthu.” Kenako anaphunzitsa ophunzira ake 70 kuti azikalalikira uthenga wabwino.

MUTU 79

Yesu Anachita Zozizwitsa Zambiri

Kulikonse kumene Yesu ankapita, kunkakhala anthu odwala oti awathandize ndipo iye ankawachiritsa. Ndiponso anaukitsa kamtsikana kena.

MUTU 80

Yesu Anasankha Atumwi 12

Kodi Yesu anawasankhiranji? Kodi mukukumbukira mayina awo?

MUTU 81

Ulaliki wa Paphiri

Yesu anaphunzitsa anthu zinthu zothandiza kwambiri.

MUTU 82

Yesu Anaphunzitsa Otsatira Ake Kupemphera

Kodi iye anawauza kuti ‘azipemphabe’ zinthu ziti?

MUTU 83

Yesu Anadyetsa Anthu Ambiri

Kodi chozizwitsa chimenechi chikutiuza chiyani za Yehova ndi Yesu?

MUTU 84

Yesu Anayenda Panyanja

Kodi mukuganiza kuti atumwi anamva bwanji ataona chozizwitsa chimenechi?

MUTU 85

Yesu Anachiritsa Munthu pa Tsiku la Sabata

N’chifukwa chiyani anthu ena sanasangalale ndi zimene Yesu anachita?

MUTU 86

Yesu Anaukitsa Lazaro

Yesu ataona Mariya akulira, nayenso analira. Koma kenako chisoni chawo chinasanduka chisangalalo.