Mawu Oyamba a Cigawo 12
Yesu anali kuphunzitsa anthu za Ufumu wa kumwamba. Anaŵaphunzitsanso kuti azipemphela kuti dzina la Mulungu liyeletsedwe, Ufumu wake ubwele, komanso kuti cifunilo cake cicitike pa dziko lapansi. Ngati ndimwe kholo, thandizani mwana wanu kumvetsa kuti pemphelo imeneyi ni yofunika kwambili kwa ise. Yesu sanalole kuti Satana amutaitse cikhulupililo cake mwa Mulungu. Yesu anasankha atumwi ake, oyamba kusankhidwa kuti akalamulile mu Ufumu wa Mulungu. M’cigawo cino, mudzaona kuti Yesu anali wodzipeleka pa kulambila koona. Cinanso, Yesu anali kukonda kuthandiza anthu. N’cifukwa cake anacilitsa odwala, kudyetsa anjala, ngakhalenso kuukitsa akufa. Mwa izi, Yesu anaonetsa zimene Ufumu wa Mulungu udzacitila anthu.
M'CIGAWO CINO
PHUNZILO 74
Pamene Yesu Anakhala Mesiya
Kodi Yohane atanthauza ciani pokamba kuti Yesu ni Mwanawankhosa wa Mulungu?
PHUNZILO 75
Mdyelekezi Ayesa Yesu
Katatu konse Mdyelekezi ayesa Yesu. Kodi ni mayeselo atatu ati amene ayesedwa nawo? Nanga Yesu ayankha bwanji?
PHUNZILO 76
Yesu Ayeletsa Kacisi
N’cifukwa ciani Yesu akuthamangitsa nyama m’kacisi, na kugubuduza mathebulo a osintha ndalama?
PHUNZILO 77
Mzimayi Akumana na Yesu pa Citsime
Mzimayi wacisamariya adabwa kuona kuti Yesu akukamba naye. Cifukwa? Kodi Yesu amuuza ciani mzimayiyo cimene sauzepo munthu aliyense?
PHUNZILO 78
Yesu Analalikila Uthenga wa Ufumu
Yesu auza ophunzila ake kukhala “asodzi a anthu.” M’kupita kwa nthawi, Yesu aphunzitsa anthu 70 nchito yolalikila uthenga wabwino.
PHUNZILO 79
Yesu Acita Zozizwitsa Zambili
Kulikonse kumene wayenda, anthu odwala abwela kwa iye kuti awacilitse, ndipo awacilitsadi. Iye aukitsa ngakhale kamtsikana kamene kamwalila.
PHUNZILO 80
Yesu Asankha Atumwi 12
Kodi Yesu wasankha atumwi 12 kuti agwile nchito yanji? Kodi ungakumbukile maina awo?
PHUNZILO 81
Ulaliki wa pa Phili
Yesu aphunzitsa mfundo zofunika kwambili ku khamu la anthu limene lasonkhana.
PHUNZILO 82
Yesu Anaphunzitsa Otsatila Ake Kupemphela
Kodi ni zinthu zotani zimene auza otsatila ake kupitiliza kupempha?
PHUNZILO 83
Yesu Anadyetsa Khamu la Anthu
Kodi cozizwitsa ici citiphunzitsa ciani za Yesu na Yehova?
PHUNZILO 84
Yesu Anayenda pa Madzi
Kodi uganiza kuti atumwi amvela bwanji pamene akuona cozizwitsa cimeneci?
PHUNZILO 86
Yesu Aukitsa Lazaro
Pamene Yesu aona Mariya akulila, nayenso ayamba kulila. Koma mwamsanga cisoni cawo cisintha kukhala cimwemwe.