Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 13

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 13

Yesu anabwera padzikoli kudzafera anthu ochimwa. Ngakhale kuti anafa, iye anagonjetsa dziko. Yehova anachita zinthu mokhulupirika ndipo anaukitsa Mwana wakeyu. Nthawi yonse imene Yesu anali padzikoli, anali wodzichepetsa, ankatumikira anthu ndipo anthuwo akalakwitsa ankawakhululukira. Yesu ataukitsidwa anapita kukaonana ndi ophunzira ake. Iye anawaphunzitsa mmene angagwirire ntchito yofunika kwambiri imene anawapatsa. Ngati ndinu kholo thandizani mwana wanu kudziwa kuti nafenso tiyenera kugwira ntchito imeneyi.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 87

Chakudya Chamadzulo Chomaliza

Yesu anapereka malangizo ofunika kwambiri kwa atumwi ake pa nthawi ya chakudya chamadzulo chomaliza.

MUTU 88

Yesu Anamangidwa

Yudasi Isikariyoti anatsogolera gulu la anthu lonyamula malupanga komanso zibonga kumunda wa Getsemani kuti akagwire Yesu.

MUTU 89

Petulo Anakana Yesu

Kodi chinachitika n’chiyani pabwalo pa nyumba ya Kayafa? Nanga n’chiyani chinkachitikira Yesu mkati mwa nyumbayo?

MUTU 90

Yesu Anaphedwa ku Gologota

N’chifukwa chiyani Pilato analamula kuti Yesu aphedwe?

MUTU 91

Yesu Anaukitsidwa

Kodi ndi zinthu zodabwitsa ziti zimene zinachitika pa masiku angapo pambuyo pa imfa ya Yesu?

MUTU 92

Yesu Anakumana ndi Asodzi

Kodi anachita chiyani kuti ayambe kukambirana nawo?

MUTU 93

Yesu Anabwerera Kumwamba

Koma asanabwerere kumwamba anapereka malangizo ofunika kwambiri kwa ophunzira ake.