Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 14

Mawu Ofotokoza Chigawo cha 14

Akhristu oyambirira analalikira uthenga wabwino wa Ufumu m’madera ambiri padzikoli. Yesu ankawatsogolera kuti adziwe kokalalikira ndiponso anawathandiza kulalikira m’zilankhulo zina. Yehova anawathandizanso kuti akhale olimba mtima komanso anawapatsa mphamvu kuti azipirira akamazunzidwa.

Yesu anaonetsa mtumwi Yohane masomphenya a ulemerero wa Yehova. M’masomphenya ena anamuonetsa Ufumu wakumwamba ukugonjetsa Satana ndiponso kumuchititsa kuti asamasocheretsenso anthu. Yohane anaona Yesu akulamulira limodzi ndi anthu 144,000. Anaonanso dziko lonse lili Paradaiso komanso anthu onse akulambira Yehova mogwirizana.

M'CHIGAWO ICHI

MUTU 94

Ophunzira a Yesu Analandira Mzimu Woyera

Kodi mzimu woyera unawapatsa mphamvu yodabwitsa yotani?

MUTU 95

Sanasiye Kulalikira

Atsogoleri achipembedzo amene anapha Yesu ankayesetsa kuletsa ophunzira ake kuti asamalalikire. Koma ophunzirawo sanasiye kulalikira.

MUTU 96

Yesu Anasankha Saulo

Saulo ankachitira nkhanza Akhristu koma anasintha.

MUTU 97

Koneliyo Analandira Mzimu Woyera

N’chifukwa chiyani Mulungu anatumiza Petulo kunyumba ya munthuyu yemwe sanali Myuda?

MUTU 98

Anthu a Mitundu Ina Anamva Uthenga Wabwino

Mtumwi Paulo ndi amishonale anzake anayamba kulalikira kumayiko akutali.

MUTU 99

Woyang’anira Ndende Anaphunzira Mawu a Yehova

Zinthu zina zimene zikutchulidwa mu nkhaniyi ndi chiwanda, chivomezi komanso lupanga.

MUTU 100

Paulo ndi Timoteyo

Anthu awiriwa akatumikira Mulungu limodzi mogwirizana kwa zaka zambiri.

MUTU 101

Paulo Anatumizidwa ku Roma

Ngakhale kuti ulendo wake unali woopsa palibe chilichonse chimene chinalepheretsa mtumwi Paulo pa ulendowo.

MUTU 102

Zimene Yohane Anaona M’masomphenya

Yesu anaonetsa Yohane masomphenya a zimene zidzachitike m’tsogolo.

MUTU 103

“Ufumu Wanu Ubwere”

Zimene Yohane anaona zimasonyeza kuti Ufumu wa Mulungu udzasintha kwambiri zinthu padzikoli.