Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 18

Tikuyamikani Cifukwa ca Dipo

Tikuyamikani Cifukwa ca Dipo

(Luka 22:20)

  1. 1. Atate Yehova

    tikuyamikani,

    Cifukwa ca cikondi

    munationetsa.

    Munapeleka mphatso

    ya Mwana wanu,

    kuti ise tikapeze

    moyo wosatha.

    (KOLASI)

    Anafela anthu onse

    kuti atipulumutse.

    Ise tidzakuyamikilani

    kwamuyaya.

  2. 2. Mwa cikondi

    Yesu anadzipeleka.

    Kufela anthu onse

    akapeze moyo.

    Mphatso imene Yesu

    anapeleka,

    imapatsa anthu onse

    ciyembekezo.

    (KOLASI)

    Anafela anthu onse

    kuti atipulumutse.

    Ise tidzakuyamikilani

    kwamuyaya.

(Onaninso Aheb. 9:13, 14; 1 Pet. 1:18, 19.)