NYIMBO 18
Tikuyamikani Cifukwa ca Dipo
(Luka 22:20)
-
1. Atate Yehova
tikuyamikani,
Cifukwa ca cikondi
munationetsa.
Munapeleka mphatso
ya Mwana wanu,
kuti ise tikapeze
moyo wosatha.
(KOLASI)
Anafela anthu onse
kuti atipulumutse.
Ise tidzakuyamikilani
kwamuyaya.
-
2. Mwa cikondi
Yesu anadzipeleka.
Kufela anthu onse
akapeze moyo.
Mphatso imene Yesu
anapeleka,
imapatsa anthu onse
ciyembekezo.
(KOLASI)
Anafela anthu onse
kuti atipulumutse.
Ise tidzakuyamikilani
kwamuyaya.
(Onaninso Aheb. 9:13, 14; 1 Pet. 1:18, 19.)