NYIMBO 18

Tikuthokoza Chifukwa cha Dipo

Tikuthokoza Chifukwa cha Dipo

(Luka 22:20)

  1. 1. Lero tabweratu,

    kwa inu Yehova,

    Chifukwa munatisonyezadi

    chikondi.

    Munapereka Mwana,

    wanu woyamba.

    Monga nsembe yoposa ina

    iliyonse.

    (KOLASI)

    Anafera anthu onse.

    Kuti tidzapulumuke.

    Tikuthokoza ndi mtima wonse,

    Inu M’lungu.

  2. 2. Mofunitsitsa Yesu

    anapereka.

    Nsembe ya dipo moti

    tikusangalala.

    Asanabwere

    kudzatipulumutsa.

    Sitinkayembekezera,

    moyo wosatha.

    (KOLASI)

    Anafera anthu onse.

    Kuti tidzapulumuke.

    Tikuthokoza ndi mtima wonse,

    Inu M’lungu.