NYIMBO 27
Ulemerero wa Ana a Mulungu Udzaonekera
-
1. Posachedwa M’lungu wathu,
Adzatisonyeza
Kuti anthu odzozedwa
Ndi ana akedi.
(KOLASI)
Khristu ndi odzozedwawo
Adzapambanadi.
Ulemerero wawonso
Udzaonekera.
-
2. Omwe atsala padziko
Adzaitanidwa.
Khristu Mfumu ya mafumu
Adzatenga onse.
(KOLASI)
Khristu ndi odzozedwawo
Adzapambanadi.
Ulemerero wawonso
Udzaonekera.
(VESI LOKOMETSERA)
Limodzi ndi Yesu Khristu
Adzamenya nkhondo.
Kenako ukwati wawo
Udzachitikadi.
(KOLASI)
Khristu ndi odzozedwawo
Adzapambanadi.
Ulemerero wawonso
Udzaonekera.
(Onaninso Dan. 2:34, 35; 1 Akor. 15:51, 52; 1 Ates. 4:15-17.)