NYIMBO 27
Ana a Mulungu Adzaonekela
(Aroma 8:19)
-
1. Nthawi yafika Yehova
Aonetse onse.
Ana ake osankhiwa
Na mzimu woyela.
(KOLASI)
Ana a Yehova M’lungu
Adzaonekela.
Pamodzi na Yesu Mfumu
Adzalamulila.
-
2. Otsalila odzozedwa
Adzaitanidwa.
Adzasonkhana pamodzi,
Na Khristu kumwamba.
(KOLASI)
Ana a Yehova M’lungu
Adzaonekela.
Pamodzi na Yesu Mfumu
Adzalamulila.
(BILIJI)
Capamodzi adzaononga
Onse oipa.
Na cimwemwe, kwa muyaya,
Adzalamulila.
(KOLASI)
Ana a Yehova M’lungu
Adzaonekela.
Pamodzi na Yesu Mfumu
Adzalamulila.
(Onaninso Dan. 2:34, 35;1 Akor. 15:51, 52; 1 Ates. 4:15-17.)