NYIMBO 30
Tate Wanga, Mulungu Wanga, Bwenzi Langa
(Aheberi 6:10)
-
1. Nthawi zina m’dzikoli,
Moyo ungakhale wovuta.
Koma ine nidziŵa
Moyo ni wabwino.
(KOLASI)
Yehova ‘tate wanga, Adziŵa kuti nimukonda.
Iye sadzanisiya; Ndipo sadzaniiŵala.
Ngakhale nivutike Iye adzanisamalila.
Yehova ni Bwenzi langa, M’lungu wanga.
-
2. Tsopano nakalamba;
Nthawi ya mavuto yafika.
Koma niyembekeza
Dziko latsopano.
(KOLASI)
Yehova ‘tate wanga, Adziŵa kuti nimukonda.
Iye sadzanisiya; Ndipo sadzaniiŵala.
Ngakhale nivutike Iye adzanisamalila.
Yehova ni Bwenzi langa, M’lungu wanga.
(Onaninso Sal. 71:17, 18.)