NYIMBO 32
Ima ku Mbali ya Yehova
(Ekisodo 32:26)
-
1. Panthawi ina ise tinali
Mbali ya cipembedzo conama.
Komabe, tinasangalaladi
Kumvela za Ufumu.
(KOLASI)
Sankhani Yehova; mumtumikile.
Sadzakusiyani; mvelani iye
Ndipo lengezani Ufumu wake.
Muŵauze onse Khristu ni Mfumu.
-
2. Tigwilizane, tilalikile
Uthenga wabwino wa Ufumu.
Nthawi yafika anthu asankhe
Kutumikila M’lungu.
(KOLASI)
Sankhani Yehova; mumtumikile.
Sadzakusiyani; mvelani iye
Ndipo lengezani Ufumu wake.
Muŵauze onse Khristu ni Mfumu.
-
3. Ise sitimayopa Satana,
Timadalila Mulungu wathu.
Ngakhale adani aculuke,
M’lungu ni mphamvu yathu.
(KOLASI)
Sankhani Yehova; mumtumikile.
Sadzakusiyani; mvelani iye
Ndipo lengezani Ufumu wake.
Muŵauze onse Khristu ni Mfumu.
(Onaninso Sal. 94:14; Miy. 3:5, 6; Aheb. 13:5.)