Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 38

Adzakulimbitsa

Adzakulimbitsa

(1 Petulo 5:10)

  1. 1. Panali chifukwa chimene Mulungu

    Anakupatsira choonadi.

    Anaona mtima wofuna kuchita

    Zabwino zomusangalatsadi.

    Unalonjeza kum’tumikira

    Ndipo iye anakuthandiza.

    (KOLASI)

    Ndi magazi a Yesu

    Anakuwombola.

    Ndiwe wa Mulungu,

    Adzakulimbitsa.

    Adzakutsogolera

    Ndi mzimu woyera.

    Adzakuteteza,

    Adzakulimbitsa.

  2. 2. Mulungu anapereka Mwana wake,

    Amafuna zizikuyendera.

    Ngati mwana wake anakupatsadi

    Sangalephere kukulimbitsa.

    Chikondi chako sangaiwale

    Ndipo sangasiye anthu ake.

    (KOLASI)

    Ndi magazi a Yesu

    Anakuwombola.

    Ndiwe wa Mulungu,

    Adzakulimbitsa.

    Adzakutsogolera

    Ndi mzimu woyera.

    Adzakuteteza,

    Adzakulimbitsa.