NYIMBO 38
Adzakulimbitsa
-
1. Panali chifukwa chimene Mulungu
Anakupatsira choonadi.
Anaona mtima wofuna kuchita
Zabwino zomusangalatsadi.
Unalonjeza kum’tumikira
Ndipo iye anakuthandiza.
(KOLASI)
Ndi magazi a Yesu
Anakuwombola.
Ndiwe wa Mulungu,
Adzakulimbitsa.
Adzakutsogolera
Ndi mzimu woyera.
Adzakuteteza,
Adzakulimbitsa.
-
2. Mulungu anapereka Mwana wake,
Amafuna zizikuyendera.
Ngati mwana wake anakupatsadi
Sangalephere kukulimbitsa.
Chikondi chako sangaiwale
Ndipo sangasiye anthu ake.
(KOLASI)
Ndi magazi a Yesu
Anakuwombola.
Ndiwe wa Mulungu,
Adzakulimbitsa.
Adzakutsogolera
Ndi mzimu woyera.
Adzakuteteza,
Adzakulimbitsa.
(Onaninso Aroma 8:32; 14:8, 9; Aheb. 6:10; 1 Pet. 2:9.)