Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 38

Adzakulimbitsa

Adzakulimbitsa

(1 Petulo 5:10)

  1. 1. Panali cifukwa cimene Yehova,

    Anakupatsila coonadi.

    Anaona kuti unali kufuna,

    Kucita zinthu zom’kondweletsa.

    Unalonjeza kum’tumikila,

    Ndipo iye anakuthandiza.

    (KOLASI)

    Na magazi a Yesu, anakuombola.

    Adzakulimbitsa, nokupatsa mphamvu.

    Adzakutsogolela, na kukuteteza.

    Adzakulimbitsa, nokupatsa mphamvu.

  2. 2. Mwana wake Yesu anamupeleka,

    Afuna zinthu zikuyendele.

    Anamupeleka Yesu mwacikondi,

    Conco Iye adzakulimbitsa.

    Cikondi cako sadzaiŵala.

    Amasamala za anthu ake.

    (KOLASI)

    Na magazi a Yesu, anakuombola.

    Adzakulimbitsa, nokupatsa mphamvu.

    Adzakutsogolela, na kukuteteza.

    Adzakulimbitsa, nokupatsa mphamvu.

(Onaninso Aroma 8:32; 14:8, 9; Aheb. 6:10; 1 Pet. 2:9.)