NYIMBO 45
Zimene Ndimaganizira Mozama
-
1. Zomwe ndimaganizira
Mozama mumtima mwanga,
Zizikusangalatsani
Kuti ndikhale wolimba.
Pamene ndili ndi nkhawa
N’kumalephera kugona,
Ndiganizire mozama
Zinthu zondilimbikitsa.
-
2. Zilizonse zolungama,
Zofunika ndi zoona,
Ndikamaziganizira
Zizindipatsa mtendere.
Nzeru zanu n’zofunika
Komanso ndi zochuluka,
Choncho ndiziganizira
Zonena zanu mozama.
(Onaninso Sal. 49:3; 63:6; 139:17, 23; Afil. 4:7, 8; 1 Tim. 4:15.)