NYIMBO 45
Kusinkhasinkha kwa Mtima Wanga
(Salimo 19:14)
-
1. Zonse za mu mtima wanga,
Zimene nimaganiza—
Zikhale zokondweletsa
Imwe Ambuye Yehova.
Pamene nili na nkhawa,
Na tulo osatuona,
Nisinkhe-sinkhe za imwe
Na pa zinthu zolungama.
-
2. Pa zilizonse zoyela,
Na zilizonse zoona,
Pa zonse zotamandika—
Ine nidzaganizila.
Maganizo anu M’lungu
Amanipatsa mtendele.
Ine niwasinkhe-sinkhe,
Pa iwo niganizile.
(Onaninso Sal. 49:3; 63:6; 139:17, 23; Afil. 4:7, 8; 1 Tim. 4:15)