NYIMBO 52
Tidzipeleke Monga Akhristu
(Aheberi 10:7, 9)
-
1. Yehova Mulungu wathu
Ni Mlengi wa zonse,
Zakumwamba na pa dziko—
Zinthu zonse n’zake.
Anatipatsanso moyo
Kuti ‘se tidziŵe
Iye ni Mulungu woona,
Tidzamutumikila.
-
2. Yesu anabatizika.
Anadzipeleka
Kutumikila Yehova,
Mpaka imfa yake.
Analonjeza Yehova,
Monga wodzozedwa,
Kuti adzamutumikila
Na moyo wake wonse.
-
3. Yehova, Atate wathu,
Ise tadzikana.
Tadzipeleka kwa imwe,
Ndise anthu anu.
Munatuma Mwana wanu,
Kuti atifele.
Na mitima yoyamikila,
Tidzalambila imwe.
(Onaninso Mat. 16:24; Maliko 8:34; Luka 9:23.)