Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

NYIMBO 59

Tamandani Ya

Tamandani Ya

(Salimo 146:2)

  1. 1. Titamande

    Ya mokweza.

    Amatipatsa zonse zabwino.

    Tsiku lonse

    Tim’tamande.

    Ndi wachikondi ndi wamphamvunso

    Ndipo tilengeze dzina lake.

  2. 2. Titamande

    Ya chifukwa

    Amatimva tikamapemphera.

    Dzanja lake

    Ndi lamphamvu.

    Amalimbikitsa ofooka.

    Timalengeza za mphamvu zake.

  3. 3. Titamande

    Ya limodzi.

    Iye ndi Mulungu wolungama.

    Adzakonza Zolakwika

    Ndipo tonse

    tidzadalitsidwa.

    Timutamande mosangalala.