NYIMBO 61
Pitani Patsogolo Mboninu
-
1. Olimba m’nthawi yamapeto ino
Ndi atumiki olengeza uthenga.
Mdyerekezi amawatsutsa,
Ndi mphamvu za Yehova samagonja.
(KOLASI)
Ndiye pitani patsogolo mboninu.
Sangalalani pogwira ntchito yake.
Uzani onse zadziko latsopano
Mmene mudzakhale madalitso.
-
2. Tisatengeke ndi moyo wofewa.
Tizipewa kusangalatsa dzikoli.
Tikane zochita za dziko
Ndi kukhala okhulupirikabe.
(KOLASI)
Ndiye pitani patsogolo mboninu.
Sangalalani pogwira ntchito yake.
Uzani onse zadziko latsopano
Mmene mudzakhale madalitso.
-
3. Ufumu wa M’lungu ukunyozedwa,
Dzina lake loyera likudetsedwa.
Tiyeni tiziliyeretsa.
Tililengeze kumitundu yonse.
(KOLASI)
Ndiye pitani patsogolo mboninu.
Sangalalani pogwira ntchito yake.
Uzani onse zadziko latsopano
Mmene mudzakhale madalitso.
(Onaninso Eks. 9:16; Afil. 1:7; 2 Tim. 2:3, 4; Yak. 1:27.)