NYIMBO 66
Lengezani Uthenga Wabwino
(Chivumbulutso 14:6, 7)
-
1. Kale anthu sanadziŵe za Ufumu.
Koma lomba na Mfumu yake tidziŵa.
Mwa cifundo cake Atate Yehova,
Anaganizila anthu ocimwafe.
Anafuna Khristu adzalamulile;
Panthawi yake,
Ufumuwo unabadwa.
Anasankha ena kudzalamulila
Pamodzi na mwana wake Khristu Mfumu.
-
2. Cinali cifuno ca Yehova M’lungu.
Kuti uthengawu ukalalikidwe.
Angelo akondwa kutsagana nafe,
Kutithandiza kulengeza Ufumu.
Ni mwayi kukhala Mboni za Yehova.
Kuyeletsa dzina lake
na kum’tamanda.
Timalemekeza nchito yathu iyi
Yolengeza uthenga kwa anthu onse.
(Onaninso Maliko 4:11; Mac. 5:31; 1 Akor. 2:1, 7.)