NYIMBO 71
Ndife Gulu Lankhondo la Yehova
-
1. Ndife gulu lankhondo
La M’lungu wathu,
Lotsogoleredwa ndi
Mwana wake Yesu.
Ngakhale titsutsidwe
Sitimasiya,
Sitiopa kanthu
Ndife olimba.
(KOLASI)
Ndife gulu lankhondo.
Tikulengeza
Ufumu wayamba
Kulamulira.
-
2. Ndife anthu a M’lungu.
Tikufufuza
Anthu omwe ndi nkhosa
Zosowa za M’lungu
Ndipo tikawapeza,
Tiwaphunzitse,
Tiwalimbikitse
Tizisonkhana.
(KOLASI)
Ndife gulu lankhondo.
Tikulengeza
Ufumu wayamba
Kulamulira.
-
3. Ndife gulu lankhondo
Lomvera Yesu,
Lokonzekera nkhondo
Ndi lolimba mtima.
Koma tikhale tcheru
Kuti tisagwe,
Zinthu zikavuta
Tisafooke.
(KOLASI)
Ndife gulu lankhondo.
Tikulengeza
Ufumu wayamba
Kulamulira.
(Onaninso Afil. 1:7; Filim. 2.)