NYIMBO 71
Ndife Asilikali a Yehova!
(Yoweli 2:7)
-
1. Ndife asilikali—
Tilalikila.
Olo Satana ‘tsutse
Ise sitileka.
Konse-konse tipita,
Kukalalika.
Timalimba mtima
Sitimayopa.
(KOLASI)
Ndife asilikali—
Timalengeza:
“Ufumu wayamba
Kulamulila.”
-
2. Ndife anthu a M’lungu—
Tifunafuna
Onse anasocela;
Ni nkhosa za M’lungu.
Ndipo tikaŵapeza
Tiŵaphunzitse,
Nakuŵaitana
Kumisonkhano.
(KOLASI)
Ndife asilikali—
Timalengeza:
“Ufumu wayamba
Kulamulila.”
-
3. Ise takonzekela
Kumenya nkhondo,
Yoteteza co’nadi
Ku mitundu yonse.
Tikhalebe olimba
Kuti tisagwe.
Zinthu zikavuta
Ticilimike.
(KOLASI)
Ndife asilikali—
Timalengeza:
“Ufumu wayamba
Kulamulila.”
(Onaninso Aef. 6:11, 14; Afil. 1:7; Fili. 2.)