NYIMBO 72
Tilalikile Coonadi ca Ufumu
(Machitidwe 20:20, 21)
-
1. Panali nthawi imene
Ise tinali mu mdima.
Yehova ‘natumiza
Kuwala kwa coonadi.
Ndipo ise tinadziŵa
Cifunilo ca Yehova.
Afuna tim’lambile
Na kulengeza za dzina lake.
Tilalika konse-konse—
Mu midzi na mu misewu.
Tigaŵila coonadi
Kwa aliyense wofuna.
Capamodzi tilengeze
Dzina la Atate wathu.
Ndipo tipitilize
Mpaka Yehova ‘tiuze: “Kwatha!”
(Onaninso Yos. 9:9; Yes. 24:15; Yoh. 8:12, 32.)