Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 75

‘Ine Nilipo, N’tumizeni

‘Ine Nilipo, N’tumizeni

(Yesaya 6:8)

  1. 1. Anthu anyoza Mulungu

    Aipitsa dzina lake.

    Zoipa zikacitika

    M’lungu ndiye wacititsa.

    Ndani adzaŵathandiza,

    Kudziŵa kuti si M’lungu?

    (KOLASI 1)

    “Ine M’lungu nitumeni,

    Nitamande dzina lanu.

    Ine nilipo n’tumizeni

    Yehova nitumeni.”

  2. 2. Ena sayopa Mulungu

    Amalambila mafano.

    Ndipo ena alambila

    Mafumu a dziko lawo.

    Ndani adzaŵacenjeza,

    Za nkhondo ya M’lungu wathu?

    (KOLASI 2)

    “Ine M’lungu nitumeni,

    nikaŵacenjeze onse.

    Ine nilipo n’tumizeni

    Yehova nitumeni.”

  3. 3. ‘Ofatsa adandaula

    Zoipa zaonjezeka.

    Na mtima wofunitsitsa

    Asakila coonadi.

    Ndani adzaŵathandiza,

    Kuti apeze co’nadi?

    (KOLASI 3)

    “Ine M’lungu nitumeni,

    Kuti nikaŵathandize.

    Ine nilipo n’tumizeni

    Yehova nitumeni.”

(Onaninso Sal. 10:4; Ezek. 9:4.)