NYIMBO 75
‘Ine Nilipo, N’tumizeni’
(Yesaya 6:8)
-
1. Anthu anyoza Mulungu
Aipitsa dzina lake.
Zoipa zikacitika
M’lungu ndiye wacititsa.
Ndani adzaŵathandiza,
Kudziŵa kuti si M’lungu?
(KOLASI 1)
“Ine M’lungu nitumeni,
Nitamande dzina lanu.
Ine nilipo n’tumizeni
Yehova nitumeni.”
-
2. Ena sayopa Mulungu
Amalambila mafano.
Ndipo ena alambila
Mafumu a dziko lawo.
Ndani adzaŵacenjeza,
Za nkhondo ya M’lungu wathu?
(KOLASI 2)
“Ine M’lungu nitumeni,
nikaŵacenjeze onse.
Ine nilipo n’tumizeni
Yehova nitumeni.”
-
3. ‘Ofatsa adandaula
Zoipa zaonjezeka.
Na mtima wofunitsitsa
Asakila coonadi.
Ndani adzaŵathandiza,
Kuti apeze co’nadi?
(KOLASI 3)
“Ine M’lungu nitumeni,
Kuti nikaŵathandize.
Ine nilipo n’tumizeni
Yehova nitumeni.”
(Onaninso Sal. 10:4; Ezek. 9:4.)