NYIMBO 78
Phunzitsani Mau a Mulungu
(Machitidwe 18:11)
-
1. Timakonda kuphunzitsa
Anthu za Yehova.
Madalitso timapeza
Ni osaneneka.
Tiphunzitse mwa cikondi
Monga Yesu Khristu
Kuti anthu onse
Ayandikile kwa Yehova.
-
2. Tiziyesetsa mwakhama
Kucita zabwino,
Kuti onse otiona
Amvele uthenga.
Zimene taphunzitsidwa
Tiphunzitse ena.
Tidzakhala acimwemwe
Tikaphunzitsa ena.
-
3. M’lungu adzatithandiza
Pophunzitsa anthu.
Tikapemphela kwa iye,
Adzatithandiza.
Tikonde onse amene
Tiphunzila nawo.
Posacedwa nawonso
Adzapita patsogolo.
(Onaninso Sal. 119:97; 2 Tim. 4:2; Tito 2:7; 1 Yoh. 5:14.)