NYIMBO 79
Aphunzitseni Kucilimika
-
1. Tikondwa kuphunzitsa anthu
Okonda coonadi.
Onani mmene akulila
M’njila ya coonadi.
(KOLASI)
Yehova, mvelani pempho
Lakuti muŵasamale
Mu dzina la Yesu Khristu
Tipemphela akhale ocilimika.
-
2. Tinali kuŵapemphelela
M’mavuto awo onse.
Tinali kuŵasamalila.
Yehova ‘wadalitsa.
(KOLASI)
Yehova, mvelani pempho
Lakuti muŵasamale
Mu dzina la Yesu Khristu
Tipemphela akhale ocilimika.
-
3. Akhale odalila M’lungu,
Na Mwana wake Yesu.
Amvele ndipo apilile,
Tifuna apambane.
(KOLASI)
Yehova, mvelani pempho
Lakuti muŵasamale
Mu dzina la Yesu Khristu
Tipemphela akhale ocilimika.
(Onaninso Luka 6:48; Mac. 5:42; Afil. 4:1.)