NYIMBO 81

Moyo wa Mpainiya

Moyo wa Mpainiya

(Mlaliki 11:6)

  1. 1. M’mawa uliwonse, tulo tisanathe,

    Timadzuka n’kupita

    kolalikira uthenga.

    Ndipo Mulungu amatitsogolera

    Timakondwa anthu

    akamamvetsera uthenga.

    (KOLASI)

    Tinasankha,

    kutumikira Yehova.

    Timachita zofuna zake.

    Tipitirizabe kulalikiraku,

    Tikatero timasonyeza

    Chikondi.

  2. 2. Pofika madzulo, timatopa ndithu,

    Komabe timapeza

    chimwemwe potumikira.

    Madalitso Yehova amatipatsa

    Nthawi zonse

    timamuthokoza potithandiza.

    (KOLASI)

    Tinasankha,

    kutumikira Yehova.

    Timachita zofuna zake.

    Tipitirizabe kulalikiraku,

    Tikatero timasonyeza

    Chikondi.