NYIMBO 86
Tiziphunzitsidwa
-
1. Bwerani mosangalala muphunzire.
“Bwerani mumwe madzi a moyo.”
Nonse anjala bwerani mudye
Ndi kudzalandira malangizo.
-
2. Tisasiyetu kusonkhana pamodzi.
Tiziphunzitsidwa ndi Mulungu.
Kuno n’kumene kuli abale,
Kuno kuli mzimu wa Mulungu.
-
3. Lilime lophunzitsidwa choonadi
Limasangalatsa kulimvera.
Tisonkhane ndi anthu a M’lungu.
Tizipezeka pamisonkhano.
(Onaninso Aheb. 10:24, 25; Chiv. 22:17.)