NYIMBO 87
Bwelani Mutsitsimulidwe!
(Aheberi 10: 24, 25)
-
1. Tili m’dziko la anthu osocela
Iwo sadziŵa co’nadi.
Kuti ’se tipewe njila zoipa,
Tifunika citsogozo.
Misonkhano imatitsitsimula,
Imatilimbikitsadi.
Itithandiza kukhulupilila
Mwa Yehova M’lungu wathu.
Conco ise sitidzataya konse
Malamulo a Yehova.
Misonkhano imatiphunzitsadi
Kukondabe coonadi.
-
2. Yehova M’lungu ni Atate wathu;
Timvele uphungu wake.
Tidzipatula nthawi yosonkhana
Kuti tikhale anzelu.
Polabadila akulu mu mpingo
Ise ticita zabwino.
Monga banja la m’cikhulupililo
Mpingo umatithandiza.
Conco pamene tiyembekezela
Tsogolo lathu lowala,
Tidzapitilizabe kuphunzila
Nzelu zocoka kumwamba.
(Onaninso Sal. 37:18; 140:1; Miy. 18:1; Aef. 5:16; Yak. 3:17.)