NYIMBO 90
Tilimbikitsane Wina na Mnzake
(Aheberi 10:24, 25)
-
1. Pamene tilimbikitsana
Kutumikila Yehova.
Cikondi cathu cimakula;
Timapezadi cimwemwe.
Cikondi timaonetsana,
Cimatilimbikitsadi.
Mpingo ni pothaŵila pathu,
Ni malo a citetezo.
-
2. Mwa mau athu acikondi
Timatonthozadi ena.
Ndipo timaŵalimbikitsa
Kuti iwo asafo’ke.
Kumatipatsadi cimwemwe
Kuseŵenzela pamodzi.
Conco tizilimbikitsana
Ndipo tizithandizana.
-
3. Tsiku la Atate Yehova,
Tidziŵa layandikadi.
Tifunika tizisonkhana
Kuti tikapulumuke.
Tiyeni tizithandizana
Kusunga umphumphu wathu.
Monga banja logwilizana
Tidzalimbikitsanadi.
(Onaninso Luka 22:32; Mac. 14: 21, 22; Agal. 6:2; 1 Ates. 5:14.)