NYIMBO 91
Ntchito Yomwe Tagwira Chifukwa cha Chikondi
-
1. Yehova tikufuna
Kupemphera mothokoza
Chifukwa mwatikonda
Potipatsa nyumbayi.
Taona mwadalitsa
Ntchito imene tagwira
Ndipo taimanga chifukwa
Mwatithandiza.
(KOLASI)
Kukumangirani nyumbayi
Yehova unali mwayi.
Tilemekeze dzina lanu nthawi zonse
Ndi kukutumikirani.
-
2. Ndife osangalala
Kuti tapeza anzathu.
Sitidzaiwala mpakana
M’Paradaiso.
Taona mzimu wanu
Chifukwa chogwirizana.
Uwu unali mwayi wokweza
Dzina lanu.
(KOLASI)
Kukumangirani nyumbayi
Yehova unali mwayi.
Tilemekeze dzina lanu nthawi zonse
Ndi kukutumikirani.
(Onaninso Sal. 116:1; 147:1; Aroma 15:6.)