Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 91

Nchito Yoonetsa Cikondi Cathu

Nchito Yoonetsa Cikondi Cathu

(Salimo 127:1)

  1. 1. Tifuna kupemphela;

    Kuti ‘se tiyamikile.

    Inu Yehova pa cikondi,

    Mwationetsa!

    Imwe mwatidalitsa,

    Pogwila nchito mwakhama.

    Takumangilani nyumbayi,

    Na manja athu.

    (KOLASI)

    Unali mwayi wapadela

    Kukumangilani nyumba.

    Tidzakutamandani M’lungu nthawi zonse

    Na kukutumikilani.

  2. 2. Ndife osangalala,

    Kuti tapeza mabwenzi!

    Tidzakumbukila nthawizi

    Ku umuyaya!

    Taona mzimu wanu,

    Pogwila nchito pamodzi.

    Dzina lanu talichukitsa;

    Kwa anthu onse!

    (KOLASI)

    Unali mwayi wapadela

    Kukumangilani nyumba.

    Tidzakutamandani M’lungu nthawi zonse

    Na kukutumikilani.

(Onaninso Sal. 116:1; 147:1; Aroma 15:6.)