NYIMBO 94
Tiyamikila Mau a Mulungu
(Afilipi 2:16)
-
1. Tikuyamikani Atate wathu,
Cifukwa mwatipatsa Mau anu.
Amatitsogolela atipatsa nzelu.
Coonadi cake catimasula.
-
2. Mau anu M’lungu, ali na mphamvu.
Akhudza zolinga za mtima wathu.
Mfundo zanu, Yehova, zitipatsa nzelu.
Zititsogolela m’zocita zathu.
-
3. Mau anu M’lungu, atithandiza.
Kuphunzila kwa aneneli anu.
Conde tithandizeni tikhale olimba.
Tikuyamikani Mulungu wathu.
(Onaninso Sal. 19:9; 119:16, 162; 2 Tim. 3:16; Yak. 5:17; 2 Pet. 1:21.)