NYIMBO 100
Alandileni na Manja Aŵili
(Machitidwe 17:7)
-
1. Yehova amatilandila bwino.
Amasamalila mosakondela.
Mvula imagwabe,
dzuŵa imawala;
Amatipatsanso cakudya.
Pamene tithandiza ovutika,
Timatengela citsanzo ca M’lungu.
Ngati tionetsa
cifundo kwa ena,
Yehova adzatidalitsa.
-
2. Pothandiza ena sitingadziŵe
Zabwino zimene tingalandile.
Ngakhale amene
sitimaŵadziŵa
Tifunika kuŵathandiza.
Monga Lidiya tiziŵalandila,
Akabwela tiziŵatsitsimula.
Atate Yehova
amaona onse
Ocitila ena cifundo.
(Onaninso Mac. 16:14, 15; Aroma 12:13; 1 Tim. 3:2; Aheb. 13:2; 1 Pet. 4:9.)