NYIMBO 102
“Muzithandiza Ofooka”
-
1. Tonse timavutika,
Timafooka,
Koma Mulungu wathu
Amatikonda.
Ali ndi chifundo
Komanso chikondi.
Nafe tikonde anthu,
Tiwathandize.
-
2. Atumiki a M’lungu
Angafooke.
Tiziwalimbikitsa
Ndi mawu athu.
Mzimu wa Mulungu
Umawalimbitsa.
Tiziwadera nkhawa
Tiwatonthoze.
-
3. M’malo mowaweruza
Tikumbukire
Kuti kukoma mtima
N’kolimbikitsa.
Tizichita khama
Powalimbikitsa.
Tikamawathandiza
Amamva bwino.
(Onaninso Yes. 35:3, 4; 2 Akor. 11:29; Agal. 6:2.)