NYIMBO 111
Zifukwa Zokhalila Acimwemwe
-
1. Zimene zitisangalatsa
Lelo zilipo zambili.
Mitundu ya anthu ibwela
Kudzalambila Yehova.
Tsiku na tsiku tiphunzila
Mau a Mulungu wathu.
Ndipo timakhulupilila
Zimene timaphunzila.
Monga moto mitima yathu
Imayaka na cimwemwe.
Olo ise timavutika
Yehova ‘matithandiza.
(KOLASI)
Yehova Mulungu wathu
Ndiyedi cimwemwe cathu.
Ubwino wake na mphamvu zake
Zimatisangalatsadi!
-
2. Timakondwela tikaona
Kumwamba, nyanja na mtunda.
Zonse Yehova analenga
Zimamutamanda iye.
Mokondwa ise tilengeza
Za Ufumu wa Mulungu.
Tilalikila konse-konse
Kuti Khristu’a lamulila.
Dziko latsopano lafika
Tiyeni tisangalale.
Tidzalandila madalitso
Na cimwemwe camuyaya.
(KOLASI)
Yehova Mulungu wathu
Ndiyedi cimwemwe cathu.
Ubwino wake na mphamvu zake
Zimatisangalatsadi!
(Onaninso Deut. 16:15; Yes. 12:6; Yoh. 15:11.)