NYIMBO 116
Mphamvu ya Kukoma Mtima
(Aefeso 4:32)
-
1. Tiyamikila imwe Yehova,
M’lungu wacikondi.
Ngakhale kuti muli na mphamvu
Ndimwedi wokoma mtima.
-
2. Mwana wanu Yesu aitana
Onse ovutika,
Kuti iwo abwele kwa iye,
Ndipo adzatonthozedwa.
-
3. Tikhale ngati M’lungu na Yesu,
Mu zocita zathu.
Ngati tikhala okoma mtima,
Tidzakhaladi amphamvu.
(Onaninso Mika 6:8; Mat. 11:28-30; Akol. 3:12; 1 Pet. 2:3.)