NYIMBO 117
Ubwino
(2 Mbiri 6:41)
-
1. O Yehova M’lungu wathu,
Ise mwatidalitsa.
Ndinu wokhulupilika
Wabwino m’zinthu zonse.
Mwationetsa cifundo
Cifukwa mutikonda.
Tidzakutumikilani
Nakukulambilani.
-
2. Tiona ubwino wanu
Mwa anthu munasankha.
Amalengeza uthenga
Na kucita zabwino.
Mwa akulu a mumpingo,
Tipita patsogolo.
Tipatseni mzimu wanu
Tionetse ubwino.
-
3. Kwa abale athu onse,
Tionetse ubwino.
Tipempha mutithandize
Kukonda athu onse.
Ku mipingo na mabanja,
Ndi kwa anansi athu,
Tipempha thandizo lanu,
Tionetse ubwino.
(Onaninso Sal. 103:10; Maliko 10:18; Agal. 5:22; Aef. 5:9.)