NYIMBO 125
“Osangalala Ndi Anthu Achifundo”
-
1. Yehova ndi wachifundo,
Amasonyeza chifundo.
Iye ndi wokoma mtima.
Amatisamaliradi.
Amamvanso mapemphero
Ochokera kwa olapa.
Amadziwa ndife fumbi,
Amatikomera mtima.
-
2. Tikachimwa n’kupemphera,
M’lungu amakhululuka.
Yesu anatiphunzitsa
Mmene tingapempherere,
Muzitikhululukira,
Takhululukira ena.
Tisasungenso zifukwa.
Tidzapezadi mtendere.
-
3. Tikapatsa ena mphatso
Tizisonyeza chifundo.
Tisamafune kutchuka
Koma kungowathandiza.
M’lungu yemwe amaona
Adzatibwezera ndithu.
Anthu onse achifundo
Mulungu amawakonda.
(Onaninso Mat. 6:2-4, 12-14.)