NYIMBO 135

Yehova Akutipempha Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzeru”

Yehova Akutipempha Kuti: “Mwana Wanga, Khala Wanzeru”

(Miyambo 27:11)

  1. 1. Mwana wanga undipatse

    mtima wako.

    Yemwe akunditonza

    aone yekha.

    Ukudziperekadi

    mofunitsitsa;

    Anthu adziwe

    kuti umandikonda.

    (KOLASI)

    Mwana wanga wokondedwawe,

    Khalatu wanzeru chonde.

    Kutitu unditumikire,

    Inde mwakufuna kwako.

  2. 2. Uzinditumikira

    mosangalala,

    Ngakhale ukapunthwa,

    ndidzakudzutsa.

    Wina ngakhale

    angakukhumudwitse,

    Usadere nkhawa

    ndidzakhala nawe.

    (KOLASI)

    Mwana wanga wokondedwawe,

    Khalatu wanzeru chonde.

    Kutitu unditumikire,

    Inde mwakufuna kwako.