NYIMBO 138
Imvi Ndi Chisoti cha Ulemerero
-
1. Pano tili ndi anthu
Achikulire.
Akukondabe M’lungu
Sanamusiye.
Ena akuvutika
Ndi umasiye.
M’lungu atonthozeni,
Alimbitseni.
(KOLASI)
Mumakumbukira
Zochita zawo.
M’lungu auzeni:
“Mwachita bwino.”
-
2. Imvi za olungama
Ndi zokongola.
Yehova M’lungu wathu
Amawakonda.
Tikumbukire kuti
Kale kalelo,
Pa unyamata wawo
Ankayesetsa.
(KOLASI)
Mumakumbukira
Zochita zawo.
M’lungu auzeni:
“Mwachita bwino.”
(Onaninso Sal. 71:9, 18; Miy. 20:29; Mat. 25:21, 23; Luka 22:28; 1 Tim. 5:1.)