NYIMBO 139
Yerekezerani Kuti Muli M’dziko Latsopano
-
1. Yerekeza ukuona
Tonse tili m’dziko latsopano.
Ona mmene udzamvere
Kukhala m’dziko lamtendere.
Oipa onse adzatha.
M’lungu wathu sadzalephera,
Adzasinthadi zinthu padzikoli.
Tidzamuimbira
nyimbo tikumati:
(KOLASI)
“Tikuthokoza mwachita bwino.
Zonse zakhaladi zatsopano.
Tikuimba nyimbo mwachisangalalo
Ndinudi woyenera ulemerero.”
-
2. Taganizira m’tsogolo
Tonse tili m’dziko latsopano.
Sitidzamva ndi kuona
Zinthu zotichititsa mantha.
Zomwe M’lungu walonjeza
Zonse zidzakwaniritsidwa.
Adzaukitsanso anthu akufa,
Iwo ndi ife
tidzamuyamikira.
(KOLASI)
“Tikuthokoza mwachita bwino.
Zonse zakhaladi zatsopano.
Tikuimba nyimbo mwachisangalalo
Ndinudi woyenera ulemerero.”
(Onaninso Sal. 37:10, 11; Yes. 65:17; Yoh. 5:28; 2 Pet. 3:13.)