NYIMBO 139
Yelekeza Uli M’dziko Latsopano
(Chivumbulutso 21:1-5)
-
1. Udzione, unione
Tili tonse m’dziko latsopano.
Ganizila za mtendele
Umene udzakhala m’dziko.
Anthu ali na cimwemwe
Mu ulamulilo wa M’lungu.
Dziko latsopano layandikila.
Na mtima wonse
tidzaimba mokondwa:
(KOLASI)
“Yehova M’lungu tiyamikila
Pa zonse imwe mwaticitila.
Mwacimwemwe ise tikuimbilani.
Zitamando na ulemu zonse n’zanu.”
-
2. Mudzione, munione,
Tili tonse m’dziko latsopano.
Zinthu zonse ni zabwino
Palibe zocititsa mantha.
Ananena, zacitika;
Monga mwa cifunilo cake.
Akufa onse adzaŵaukitsa;
Capamodzi
tidzaimbila Yehova:
(KOLASI)
“Yehova M’lungu tiyamikila
Pa zonse imwe mwaticitila.
Mwacimwemwe ise tikuimbilani.
Zitamando na ulemu zonse n’zanu.”
(Onaninso Sal. 37:10, 11; Yes. 65:17; Yoh. 5:28; 2 Pet. 3:13.)