Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 139

Yelekeza Uli M’dziko Latsopano

Yelekeza Uli M’dziko Latsopano

(Chivumbulutso 21:1-5)

  1. 1. Udzione, unione

    Tili tonse m’dziko latsopano.

    Ganizila za mtendele

    Umene udzakhala m’dziko.

    Anthu ali na cimwemwe

    Mu ulamulilo wa M’lungu.

    Dziko latsopano layandikila.

    Na mtima wonse

    tidzaimba mokondwa:

    (KOLASI)

    “Yehova M’lungu tiyamikila

    Pa zonse imwe mwaticitila.

    Mwacimwemwe ise tikuimbilani.

    Zitamando na ulemu zonse n’zanu.”

  2. 2. Mudzione, munione,

    Tili tonse m’dziko latsopano.

    Zinthu zonse ni zabwino

    Palibe zocititsa mantha.

    Ananena, zacitika;

    Monga mwa cifunilo cake.

    Akufa onse adzaŵaukitsa;

    Capamodzi

    tidzaimbila Yehova:

    (KOLASI)

    “Yehova M’lungu tiyamikila

    Pa zonse imwe mwaticitila.

    Mwacimwemwe ise tikuimbilani.

    Zitamando na ulemu zonse n’zanu.”

(Onaninso Sal. 37:10, 11; Yes. 65:17; Yoh. 5:28; 2 Pet. 3:13.)