Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

NYIMBO 141

Moyo ni Cozizwitsa

Moyo ni Cozizwitsa

(Salimo 36:9)

  1. 1. Yehova M’lungu amatipatsa,

    Mphatso zotithandiza mu umoyo—

    Dzuŵa na mvula, mwana wobadwa.

    Zonse ni mphatso Yehova atipatsa.

    (KOLASI)

    Timayamikila mphatso ya moyo

    Na kukondanso amene anatipatsa.

    Mphatsoyi ya moyo niyodabwitsadi.

    Inde, mphatso iyi—niyapadeladi.

  2. 2. Tikavutika tingaganize

    Kuti moyo ulibe tanthauzo.

    Koma tidziŵa moyo ni mphatso.

    Tiyamikila kuti tili na moyo.

    (KOLASI)

    Timayamikila mphatso ya moyo.

    Timaonetsanso cikondi kwa anzathu.

    Mphatsoyi ya moyo niyodabwitsadi.

    Inde mphatso iyi—niyapadeladi.

(Onaninso Yobu 2:9; Sal. 34:12; Mlal. 8:15; Mat. 22:37-40; Aroma 6:23)