NYIMBO 143
Musaleke Kugwila Nchito, Kuyang’anila, na Kuyembekezela
(Aroma 8: 20-25)
-
1. M’lungu wa nyengo na nthawi,
Dzina lake ni Yehova.
Posacedwa ‘dzayeletsa
Dzina lake loyela.
(KOLASI)
Moyo udzakhala wacimwemwe,
Pano padziko lapansi.
M’lungu watilonjeza.
-
2. Iye anakonza nthawi;
Yakuti Yesu abwele
Kudzacotsa ‘nthu oipa
Ndipo adzapambana.
(KOLASI)
Moyo udzakhala wacimwemwe,
Pano padziko lapansi.
M’lungu watilonjeza.
-
3. Olo tivutike bwanji,
Tidziŵa kuti Yehova,
Adzatipulumutsadi,
Na kuthetsa mavuto.
(KOLASI)
Moyo udzakhala wacimwemwe,
Pano padziko lapansi.
M’lungu watilonjeza.
(Onaninso Mat. 25:13; Luka 12:36.)